Zefaniya 2
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
2 Sonkhanani pamodzi, sonkhanani pamodzi,
inu mtundu wochititsa manyazi,
2 isanafike nthawi yachiweruzo,
nthawi yanu isanawuluke ngati mungu,
usanakufikeni mkwiyo woopsa wa Yehova,
tsiku la ukali wa Yehova lisanafike pa inu.
3 Funafunani Yehova, inu nonse odzichepetsa a mʼdziko,
inu amene mumachita zimene amakulamulani.
Funafunani chilungamo, funafunani kudzichepetsa;
mwina mudzatetezedwa
pa tsiku la mkwiyo wa Yehova.
Za Afilisti
4 Gaza adzasiyidwa
ndipo Asikeloni adzasanduka bwinja.
Nthawi yamasana Asidodi adzakhala wopanda anthu
ndipo Ekroni adzazulidwa.
5 Tsoka inu okhala mʼmbali mwa nyanja,
inu mtundu wa Akereti;
mawu a Yehova akutsutsa
iwe Kanaani, dziko la Afilisti.
“Ndidzakuwononga
ndipo palibe amene adzatsale.”
6 Dziko la mʼmbali mwa nyanja, kumene kumakhala Akereti,
lidzakhala malo a abusa ndi la makola a nkhosa.
7 Malowa adzakhala a anthu otsala a nyumba ya Yuda;
adzapezako msipu.
Nthawi ya madzulo adzagona
mʼnyumba za Asikeloni.
Yehova Mulungu wawo adzawasamalira;
adzabwezeretsa mtendere wawo.
Za Mowabu ndi Amoni
8 “Ndamva kunyoza kwa Mowabu
ndi chipongwe cha Amoni,
amene ananyoza anthu anga
ndi kuopseza kuti alanda dziko lawo.
9 Choncho, pali Ine Wamoyo,”
akutero Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli,
“Ndithu, Mowabu adzasanduka ngati Sodomu,
Amoni adzasanduka ngati Gomora;
malo a zomeramera ndi maenje a mchere,
dziko la bwinja mpaka muyaya.
Anthu anga otsala adzawafunkha;
opulumuka a mtundu wanga adzalandira dziko lawo.”
10 Ichi ndi chimene adzalandire chifukwa cha kunyada kwawo,
chifukwa chonyoza ndi kuchitira chipongwe anthu a Yehova Wamphamvuzonse.
11 Yehova adzawachititsa mantha kwambiri
pamene adzawononga milungu yonse ya mʼdzikomo.
Ndipo mitundu ya anthu pa dziko lonse idzamulambira,
uliwonse ku dziko la kwawo.
Za Kusi
12 “Inunso anthu a ku Kusi,
mudzaphedwa ndi lupanga.”
Za Asiriya
13 Yehova adzatambasulira dzanja lake kumpoto
ndi kuwononga Asiriya,
kusiya Ninive atawonongekeratu
ndi owuma ngati chipululu.
14 Nkhosa ndi ngʼombe zidzagona pansi kumeneko,
pamodzi ndi nyama zakuthengo za mtundu uliwonse.
Akadzidzi a mʼchipululu ndi akanungu
adzakhala pa nsanamira zake.
Kulira kwawo kudzamveka mʼmazenera,
mʼmakomo mwawo mudzakhala zinyalala zokhazokha,
nsanamira za mkungudza zidzakhala poonekera.
15 Umenewu ndiye mzinda wosasamala
umene kale unali wotetezedwa.
Unkanena kuti mu mtima mwake,
“Ine ndine, ndipo palibenso wina wondiposa.”
Taonani lero wasanduka bwinja,
kokhala nyama zakutchire!
Onse owudutsa akuwunyoza
ndi kupukusa mitu yawo.
Zephaniah 2
English Standard Version
Judgment on Judah's Enemies
2 Gather together, yes, gather,
O (A)shameless nation,
2 (B)before the decree takes effect[a]
—before the day passes away (C)like chaff—
(D)before there comes upon you
the burning anger of the Lord,
before there comes upon you
the day of the anger of the Lord.
3 (E)Seek the Lord, (F)all you humble of the land,
who do his just commands;[b]
(G)seek righteousness; seek humility;
(H)perhaps (I)you may be hidden
on the day of the anger of the Lord.
4 (J)For Gaza shall be deserted,
and Ashkelon shall become a desolation;
Ashdod's people shall be driven out at noon,
and Ekron shall be uprooted.
5 Woe to (K)you inhabitants of the seacoast,
you nation of (L)the Cherethites!
(M)The word of the Lord is against you,
(N)O Canaan, land of the Philistines;
and I will destroy you (O)until no inhabitant is left.
6 (P)And you, O seacoast, (Q)shall be pastures,
with meadows[c] for shepherds
and folds for flocks.
7 (R)The seacoast shall become the possession
of (S)the remnant of the house of Judah,
(T)on which they shall graze,
and in the houses of Ashkelon
they shall lie down at evening.
For the Lord their God (U)will be mindful of them
and (V)restore their fortunes.
8 “I have heard (W)the taunts of Moab
and (X)the revilings of the Ammonites,
how they have taunted my people
and made boasts (Y)against their territory.
9 Therefore, (Z)as I live,” declares the Lord of hosts,
the God of Israel,
“Moab shall become (AA)like Sodom,
and the Ammonites (AB)like Gomorrah,
a land possessed by nettles and salt pits,
and a waste forever.
The remnant of my people shall plunder them,
and the survivors of my nation shall possess them.”
10 This shall be their lot in return (AC)for their pride,
because they taunted and boasted
against the people of the Lord of hosts.
11 The Lord will be awesome against them;
(AD)for he will famish all the gods of the earth,
and (AE)to him shall bow down,
each in its place,
all (AF)the lands of the nations.
12 (AG)You also, O Cushites,
shall be slain by my sword.
13 And he will stretch out his hand against the north
(AH)and destroy Assyria,
and he (AI)will make Nineveh a desolation,
a dry waste like the desert.
14 (AJ)Herds shall lie down in her midst,
all kinds of beasts;[d]
(AK)even the owl and the hedgehog[e]
shall lodge in her capitals;
a voice shall hoot in the window;
devastation will be on the threshold;
for (AL)her cedar work will be laid bare.
15 This is the exultant city
(AM)that lived securely,
that said in her heart,
“I am, and there is no one else.”
What a desolation she has become,
(AN)a lair for wild beasts!
(AO)Everyone who passes by her
hisses and (AP)shakes his fist.
Footnotes
- Zephaniah 2:2 Hebrew gives birth
- Zephaniah 2:3 Or who carry out his judgment
- Zephaniah 2:6 Or caves
- Zephaniah 2:14 Hebrew beasts of every nation
- Zephaniah 2:14 The identity of the animals rendered owl and hedgehog is uncertain
Zephaniah 2
New International Version
Judah and Jerusalem Judged Along With the Nations
Judah Summoned to Repent
2 Gather together,(A) gather yourselves together,
you shameful(B) nation,
2 before the decree takes effect
and that day passes like windblown chaff,(C)
before the Lord’s fierce anger(D)
comes upon you,
before the day of the Lord’s wrath(E)
comes upon you.
3 Seek(F) the Lord, all you humble of the land,
you who do what he commands.
Seek righteousness,(G) seek humility;(H)
perhaps you will be sheltered(I)
on the day of the Lord’s anger.
Philistia
4 Gaza(J) will be abandoned
and Ashkelon(K) left in ruins.
At midday Ashdod will be emptied
and Ekron uprooted.
5 Woe to you who live by the sea,
you Kerethite(L) people;
the word of the Lord is against you,(M)
Canaan, land of the Philistines.
He says, “I will destroy you,
and none will be left.”(N)
6 The land by the sea will become pastures
having wells for shepherds
and pens for flocks.(O)
7 That land will belong
to the remnant(P) of the people of Judah;
there they will find pasture.
In the evening they will lie down
in the houses of Ashkelon.
The Lord their God will care for them;
he will restore their fortunes.[a](Q)
Moab and Ammon
8 “I have heard the insults(R) of Moab(S)
and the taunts of the Ammonites,(T)
who insulted(U) my people
and made threats against their land.(V)
9 Therefore, as surely as I live,”
declares the Lord Almighty,
the God of Israel,
“surely Moab(W) will become like Sodom,(X)
the Ammonites(Y) like Gomorrah—
a place of weeds and salt pits,
a wasteland forever.
The remnant of my people will plunder(Z) them;
the survivors(AA) of my nation will inherit their land.(AB)”
10 This is what they will get in return for their pride,(AC)
for insulting(AD) and mocking
the people of the Lord Almighty.(AE)
11 The Lord will be awesome(AF) to them
when he destroys all the gods(AG) of the earth.(AH)
Distant nations will bow down to him,(AI)
all of them in their own lands.
Cush
Assyria
13 He will stretch out his hand against the north
and destroy Assyria,(AL)
leaving Nineveh(AM) utterly desolate
and dry as the desert.(AN)
14 Flocks and herds(AO) will lie down there,
creatures of every kind.
The desert owl(AP) and the screech owl(AQ)
will roost on her columns.
Their hooting will echo through the windows,
rubble will fill the doorways,
the beams of cedar will be exposed.
15 This is the city of revelry(AR)
that lived in safety.(AS)
She said to herself,
“I am the one! And there is none besides me.”(AT)
What a ruin she has become,
a lair for wild beasts!(AU)
All who pass by her scoff(AV)
and shake their fists.(AW)
Footnotes
- Zephaniah 2:7 Or will bring back their captives
- Zephaniah 2:12 That is, people from the upper Nile region
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
The ESV® Bible (The Holy Bible, English Standard Version®), © 2001 by Crossway, a publishing ministry of Good News Publishers. ESV Text Edition: 2025.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.

