Add parallel Print Page Options

17 “Mtima wanga wasweka,
    masiku anga atha,
    manda akundidikira.
Ndithudi, anthu ondiseka andizungulira;
    maso anga akupenyetsetsa mdani wanga.

“Inu Mulungu, patseni chikole chimene mukufuna.
    Ndani wina amene adzandiperekera ine chikole?
Inu mwatseka maganizo awo kuti asamvetse zinthu;
    choncho simudzawalola kuti apambane.
Ngati munthu apereka mnzake chifukwa cha chuma,
    ana ake sadzaona mwayi.

“Mulungu wandisandutsa chisudzo chochiseka aliyense,
    munthu amene anthu amalavulira malovu nkhope yake.
Mʼmaso mwanga mwada ndi chisoni;
    ndawonda ndi mutu womwe.
Anthu olungama akudabwa nazo zimenezi;
    anthu osachimwa akupsera mtima anthu osapembedza Mulungu.
Komabe anthu olungama adzasunga njira zawo,
    ndipo anthu a makhalidwe abwino mphamvu zawo zidzanka zikuchuluka.

10 “Tsono bwerani nonsenu, bwerezaninso mawu anuwo,
    sindidzapezapo munthu wanzeru pakati panupo.
11 Masiku anga atha, zimene ndinakonza zalephereka,
    pamodzinso ndi zokhumba za mtima wanga.
12 Anthu awa amasandutsa usiku kukhala usana,
    nthawi ya usiku iwo amati ‘kwatsala pangʼono kucha.’
13 Ngati nyumba imene ndikuyiyembekezera ndi manda,
    ngati ndiyala bedi langa mu mdima,
14 ngati ndinena kwa dzenje la manda ‘ndinu abambo anga,’
    ndiponso kwa mphutsi kuti, ‘ndinu amayi anga’ kapena ‘mlongo wanga,’
15 tsono chiyembekezo changa chili kuti?
    Ndani angaone populumukira panga?
16 Ndithu sindidzakhalanso ndi chiyembekezo chilichonse,
    polowa mʼmanda, pamene ndidzatsikira ku fumbi.”

17 My spirit(A) is broken,
    my days are cut short,(B)
    the grave awaits me.(C)
Surely mockers(D) surround me;(E)
    my eyes must dwell on their hostility.

“Give me, O God, the pledge you demand.(F)
    Who else will put up security(G) for me?(H)
You have closed their minds to understanding;(I)
    therefore you will not let them triumph.
If anyone denounces their friends for reward,(J)
    the eyes of their children will fail.(K)

“God has made me a byword(L) to everyone,(M)
    a man in whose face people spit.(N)
My eyes have grown dim with grief;(O)
    my whole frame is but a shadow.(P)
The upright are appalled at this;
    the innocent are aroused(Q) against the ungodly.
Nevertheless, the righteous(R) will hold to their ways,
    and those with clean hands(S) will grow stronger.(T)

10 “But come on, all of you, try again!
    I will not find a wise man among you.(U)
11 My days have passed,(V) my plans are shattered.
    Yet the desires of my heart(W)
12 turn night into day;(X)
    in the face of the darkness light is near.(Y)
13 If the only home I hope for is the grave,(Z)
    if I spread out my bed(AA) in the realm of darkness,(AB)
14 if I say to corruption,(AC) ‘You are my father,’
    and to the worm,(AD) ‘My mother’ or ‘My sister,’
15 where then is my hope—(AE)
    who can see any hope for me?(AF)
16 Will it go down to the gates of death?(AG)
    Will we descend together into the dust?”(AH)