Add parallel Print Page Options

52 Dzambatuka, dzambatuka iwe Ziyoni,
    vala zilimbe.
Vala zovala zako zokongola,
    iwe Yerusalemu, mzinda wopatulika.
Pakuti kuyambira tsopano anthu osachita mdulidwe ndi odetsedwa
    sadzalowanso pa zipata zako.
Sasa fumbi lako;
    imirira nukhale pa mpando waufumu, iwe Yerusalemu.
Inu omangidwa a ku Ziyoni,
    masulani maunyolo amene ali mʼkhosi mwanumo.

Pakuti Yehova akuti,

“Sindinalandirepo kanthu pamene ndinakugulitsani,
    choncho mudzawomboledwa wopanda ndalama.”

Pakuti Ambuye Yehova akuti,

“Poyamba paja anthu anga anapita kukakhala ku Igupto;
    nawonso Asiriya awapondereza popanda chifukwa.”

Tsopano Ine Yehova ndikuti,

“Kodi nditani pakuti anthu anga atengedwa ukapolo osaperekapo kanthu,
    amene amawalamulira amawanyoza,”
            akutero Yehova.
“Ndipo tsiku lonse, akungokhalira
    kuchita chipongwe dzina langa.
Tsono tsiku limenelo anthu anga adzadziwa dzina langa;
    kotero adzadziwa
kuti ndi Ine amene ndikuyankhula,
    Indedi, ndine.”

Ngokongoladi mapazi a
    amithenga obweretsa nkhani yabwino amene akuyenda pa mapiri.
Iwo akukubweretserani nkhani zabwino za mtendere,
    chisangalalo ndi chipulumutso.
    Iwo akubwera kudzawuza anthu
a ku Ziyoni kuti,
    “Mulungu wako ndi mfumu!”
Mverani! Alonda anu akukweza mawu awo;
    akuyimba pamodzi mwachimwemwe.
Popeza akuona chamaso
    kubwera kwa Yehova ku Yerusalemu.
Imbani pamodzi mofuwula nyimbo zachimwemwe,
    inu mabwinja a Yerusalemu,
pakuti Yehova watonthoza mtima anthu ake,
    wapulumutsa Yerusalemu.
10 Yehova wagwiritsa ntchito mphamvu zake zopatulika
    pamaso pa anthu a mitundu yonse,
ndipo anthu onse a dziko lapansi
    adzaona chipulumutso cha Mulungu wathu.

11 Nyamukani, nyamukani, chokaniko ku Babuloniko!
    Musakhudze kanthu kodetsedwa!
Inu amene mumanyamula ziwiya za Yehova
    tulukanimo ndipo mudziyeretse.
12 Koma simudzachoka mofulumira
    kapena kuchita chothawa;
pakuti Yehova adzayenda patsogolo panu,
    Mulungu wa Israeli adzakutetezani kumbuyo kwanu.

Kuzunzika ndi Ulemerero wa Mtumiki

13 Taonani, mtumiki wanga adzapambana pa ntchito yake
    adzakwezedwa ndi kulemekezedwa ndipo adzalandira ulemu waukulu kwambiri.
14 Anthu ambiri atamuona anadzidzimuka,
    chifukwa nkhope yake inali itasakazika; sinalinso ngati ya munthu.
    Ndipo thupi lake linasakazika; silinalinso ngati la munthu.
15 Momwemonso anthu a mitundu yonse adzadodoma naye,
    ndipo mafumu adzatseka pakamwa pawo kusowa chonena chifukwa cha iye.
Pakuti zinthu zimene iwo sanawuzidwepo, adzaziona,
    ndipo zimene sanazimvepo, adzazimvetsa.

52 Awake, awake,(A) Zion,
    clothe yourself with strength!(B)
Put on your garments of splendor,(C)
    Jerusalem, the holy city.(D)
The uncircumcised(E) and defiled(F)
    will not enter you again.(G)
Shake off your dust;(H)
    rise up,(I) sit enthroned, Jerusalem.
Free yourself from the chains on your neck,(J)
    Daughter Zion,(K) now a captive.

For this is what the Lord says:

“You were sold for nothing,(L)
    and without money(M) you will be redeemed.(N)

For this is what the Sovereign Lord says:

“At first my people went down to Egypt(O) to live;
    lately, Assyria(P) has oppressed them.

“And now what do I have here?” declares the Lord.

“For my people have been taken away for nothing,
    and those who rule them mock,[a]
declares the Lord.
“And all day long
    my name is constantly blasphemed.(Q)
Therefore my people will know(R) my name;(S)
    therefore in that day(T) they will know
that it is I who foretold(U) it.
    Yes, it is I.”

How beautiful on the mountains(V)
    are the feet of those who bring good news,(W)
who proclaim peace,(X)
    who bring good tidings,
    who proclaim salvation,
who say to Zion,
    “Your God reigns!”(Y)
Listen! Your watchmen(Z) lift up their voices;(AA)
    together they shout for joy.(AB)
When the Lord returns(AC) to Zion,(AD)
    they will see it with their own eyes.
Burst into songs of joy(AE) together,
    you ruins(AF) of Jerusalem,
for the Lord has comforted(AG) his people,
    he has redeemed Jerusalem.(AH)
10 The Lord will lay bare his holy arm(AI)
    in the sight of all the nations,(AJ)
and all the ends of the earth(AK) will see
    the salvation(AL) of our God.

11 Depart,(AM) depart, go out from there!
    Touch no unclean thing!(AN)
Come out from it and be pure,(AO)
    you who carry the articles(AP) of the Lord’s house.
12 But you will not leave in haste(AQ)
    or go in flight;
for the Lord will go before you,(AR)
    the God of Israel will be your rear guard.(AS)

The Suffering and Glory of the Servant

13 See, my servant(AT) will act wisely[b];
    he will be raised and lifted up and highly exalted.(AU)
14 Just as there were many who were appalled(AV) at him[c]
    his appearance was so disfigured(AW) beyond that of any human being
    and his form marred beyond human likeness(AX)
15 so he will sprinkle(AY) many nations,[d]
    and kings(AZ) will shut their mouths(BA) because of him.
For what they were not told, they will see,
    and what they have not heard, they will understand.(BB)

Footnotes

  1. Isaiah 52:5 Dead Sea Scrolls and Vulgate; Masoretic Text wail
  2. Isaiah 52:13 Or will prosper
  3. Isaiah 52:14 Hebrew you
  4. Isaiah 52:15 Or so will many nations be amazed at him (see also Septuagint)