Add parallel Print Page Options

Tsoka kwa Mzinda wa Davide

29 Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli,
    mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo!
Papite chaka chimodzi kapena ziwiri
    ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli
    ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula,
    mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo;
    ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo
    ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka,
    mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi,
adzamveka ngati a mzukwa.
    Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.

Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti.
    Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo.
Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
    Yehova Wamphamvuzonse adzabwera
ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu,
    kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli
    nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga,
chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto,
    gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya,
    koma podzuka ali nayobe njala;
kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa,
    koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa.
Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse
    chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.

Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa.
    Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya,
ledzerani, koma osati ndi vinyo,
    dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 Yehova wakugonetsani tulo tofa nato.
    Watseka maso anu, inu aneneri;
    waphimba mitu yanu, inu alosi.

11 Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.” 12 Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”

13 Ambuye akuti,

“Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo,
    ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo,
    koma mitima yawo ili kutali ndi Ine.
Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso.
    Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira
    kuwachitira ntchito zodabwitsa;
nzeru za anthu anzeru zidzatha,
    luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Tsoka kwa amene amayesetsa
    kubisira Yehova maganizo awo,
amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti,
    “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Inu mumazondotsa zinthu
    ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya.
Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti
    “Sunandipange ndi iwe?”
Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti,
    “Iwe sudziwa chilichonse?”

17 Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde,
    ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku,
    ndipo anthu osaona amene
    ankakhala mu mdima adzapenya.
19 Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova;
    ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 Koma anthu ankhanza adzazimirira,
    oseka anzawo sadzaonekanso,
    ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa,
    kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu
    ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.

22 Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti,

“Anthu anga sadzachitanso manyazi;
    nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 Akadzaona ana awo ndi
    ntchito ya manja anga pakati pawo,
adzatamanda dzina langa loyera;
    adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo,
    ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Anthu opusa adzapeza nzeru;
    onyinyirika adzalandira malangizo.”

Woe to David’s City

29 Woe(A) to you, Ariel, Ariel,(B)
    the city(C) where David settled!
Add year to year
    and let your cycle of festivals(D) go on.
Yet I will besiege Ariel;(E)
    she will mourn and lament,(F)
    she will be to me like an altar hearth.[a](G)
I will encamp against you on all sides;
    I will encircle(H) you with towers
    and set up my siege works(I) against you.
Brought low, you will speak from the ground;
    your speech will mumble(J) out of the dust.(K)
Your voice will come ghostlike(L) from the earth;
    out of the dust your speech will whisper.(M)

But your many enemies will become like fine dust,(N)
    the ruthless(O) hordes like blown chaff.(P)
Suddenly,(Q) in an instant,
    the Lord Almighty will come(R)
with thunder(S) and earthquake(T) and great noise,
    with windstorm and tempest(U) and flames of a devouring fire.(V)
Then the hordes of all the nations(W) that fight against Ariel,(X)
    that attack her and her fortress and besiege her,
will be as it is with a dream,(Y)
    with a vision in the night—
as when a hungry person dreams of eating,
    but awakens(Z) hungry still;
as when a thirsty person dreams of drinking,
    but awakens faint and thirsty still.(AA)
So will it be with the hordes of all the nations
    that fight against Mount Zion.(AB)

Be stunned and amazed,(AC)
    blind yourselves and be sightless;(AD)
be drunk,(AE) but not from wine,(AF)
    stagger,(AG) but not from beer.
10 The Lord has brought over you a deep sleep:(AH)
    He has sealed your eyes(AI) (the prophets);(AJ)
    he has covered your heads (the seers).(AK)

11 For you this whole vision(AL) is nothing but words sealed(AM) in a scroll. And if you give the scroll to someone who can read, and say, “Read this, please,” they will answer, “I can’t; it is sealed.” 12 Or if you give the scroll to someone who cannot read, and say, “Read this, please,” they will answer, “I don’t know how to read.”

13 The Lord says:

“These people(AN) come near to me with their mouth
    and honor me with their lips,(AO)
    but their hearts are far from me.(AP)
Their worship of me
    is based on merely human rules they have been taught.[b](AQ)
14 Therefore once more I will astound these people
    with wonder upon wonder;(AR)
the wisdom of the wise(AS) will perish,
    the intelligence of the intelligent will vanish.(AT)
15 Woe to those who go to great depths
    to hide(AU) their plans from the Lord,
who do their work in darkness and think,
    “Who sees us?(AV) Who will know?”(AW)
16 You turn things upside down,
    as if the potter were thought to be like the clay!(AX)
Shall what is formed say to the one who formed(AY) it,
    “You did not make me”?
Can the pot say to the potter,(AZ)
    “You know nothing”?(BA)

17 In a very short time,(BB) will not Lebanon(BC) be turned into a fertile field(BD)
    and the fertile field seem like a forest?(BE)
18 In that day(BF) the deaf(BG) will hear the words of the scroll,
    and out of gloom and darkness(BH)
    the eyes of the blind will see.(BI)
19 Once more the humble(BJ) will rejoice in the Lord;
    the needy(BK) will rejoice in the Holy One(BL) of Israel.
20 The ruthless(BM) will vanish,(BN)
    the mockers(BO) will disappear,
    and all who have an eye for evil(BP) will be cut down—
21 those who with a word make someone out to be guilty,
    who ensnare the defender in court(BQ)
    and with false testimony(BR) deprive the innocent of justice.(BS)

22 Therefore this is what the Lord, who redeemed(BT) Abraham,(BU) says to the descendants of Jacob:

“No longer will Jacob be ashamed;(BV)
    no longer will their faces grow pale.(BW)
23 When they see among them their children,(BX)
    the work of my hands,(BY)
they will keep my name holy;(BZ)
    they will acknowledge the holiness of the Holy One(CA) of Jacob,
    and will stand in awe of the God of Israel.
24 Those who are wayward(CB) in spirit will gain understanding;(CC)
    those who complain will accept instruction.”(CD)

Footnotes

  1. Isaiah 29:2 The Hebrew for altar hearth sounds like the Hebrew for Ariel.
  2. Isaiah 29:13 Hebrew; Septuagint They worship me in vain; / their teachings are merely human rules