Yeremiya 47
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Uthenga Wonena za Afilisti
47 Uthenga umene Yehova anamupatsa mneneri Yeremiya wonena za Afilisti, Farao asanathire nkhondo Gaza ndi uwu:
2 Yehova akuti,
“Taonani mmene madzi akubwerera kuchokera kumpoto;
adzasanduka mtsinje wosefukira ndi a mkokomo.
Adzasefukira mʼdziko monse ndi kumiza chilichonse mʼmenemo,
mizinda ndi onse okhala mʼmenemo.
Anthu adzafuwula;
anthu onse okhala mʼdzikomo adzalira
3 akadzamva mgugu wa ngʼombe zazimuna zothamanga,
phokoso la magaleta ake
ndi kulira kwa mikombero yake.
Makolo sadzatembenuka kuti athandize ana awo;
manja awo adzangoti khoba.
4 Pakuti tsiku lafika
lowononga Afilisti onse
ndi kupha onse otsala,
onse amene akanatha kuthandiza Turo ndi Sidoni.
Yehova ali pafupi kuwononga Afilisti,
otsala ochokera ku zilumba za ku Kafitori.
5 Anthu a ku Gaza ameta mipala;
anthu a ku Asikeloni akhala chete.
Inu otsala a ku chigwa,
mudzakhala mukudzichekacheka mpaka liti?
6 “Mukulira kuti, ‘Aa, lupanga la Yehova,
kodi udzapumula liti?
Bwerera mʼmalo ako;
ukhale momwemo ndipo ukhale chete.’
7 Koma lupangalo lidzapumula bwanji
pamene Yehova walilamulira
kuti lithire nkhondo
Asikeloni ndi anthu a mʼmbali mwa nyanja?”
Jeremiah 47
New International Version
A Message About the Philistines
47 This is the word of the Lord that came to Jeremiah the prophet concerning the Philistines(A) before Pharaoh attacked Gaza:(B)
2 This is what the Lord says:
“See how the waters are rising in the north;(C)
they will become an overflowing torrent.
They will overflow the land and everything in it,
the towns and those who live in them.
The people will cry out;
all who dwell in the land will wail(D)
3 at the sound of the hooves of galloping steeds,
at the noise of enemy chariots(E)
and the rumble of their wheels.
Parents will not turn to help their children;
their hands will hang limp.(F)
4 For the day has come
to destroy all the Philistines
and to remove all survivors
who could help Tyre(G) and Sidon.(H)
The Lord is about to destroy the Philistines,(I)
the remnant from the coasts of Caphtor.[a](J)
5 Gaza will shave(K) her head in mourning;
Ashkelon(L) will be silenced.
You remnant on the plain,
how long will you cut(M) yourselves?
Footnotes
- Jeremiah 47:4 That is, Crete
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.