Numeri 32
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Mafuko a ku Tsidya la Yorodani
32 Arubeni ndi Agadi amene anali ndi ngʼombe zambiri ndi ziweto zina anaona dziko la Yazeri ndi la Giliyadi kuti linali labwino kwa ziwetozo. 2 Choncho Arubeni ndi Agadi anapita kwa Mose ndi kwa wansembe Eliezara ndi kwa atsogoleri a anthu ndi kunena kuti, 3 “Ataroti, Diboni, Yazeri, Nimira, Hesiboni, Eleali, Sebamu, Nebo ndi Beoni, 4 dziko lomwe Yehova anagonjetsa pamaso pa Aisraeli, ndiwo malo woyenera ziweto, ndipo atumiki anufe tili ndi ziweto. 5 Iwo anati, ‘Ngati tapeza ufulu pamaso panu atumiki anufe, mutipatse dziko limeneli kuti likhale lathu. Tisawoloke nanu Yorodani.’ ”
6 Ndipo Mose anati kwa Agadi ndi Arubeni, “Kodi anthu a mtundu wanu apite ku nkhondo inu mutangokhala kuno? 7 Chifukwa chiyani mukufowoketsa Aisraeli kupita mʼdziko limene Yehova wawapatsa? 8 Izi ndi zimene makolo anu anachita pamene ndinawatuma kuchokera ku Kadesi kukaona dzikolo. 9 Atapita ku chigwa cha Esikolo, ndi kuliona dzikolo, anafowoketsa Aisraeli kuti asalowe mʼdziko limene Yehova anawapatsa. 10 Yehova anakwiya tsiku limenelo ndipo analumbira kuti, 11 ‘Chifukwa sananditsatire ndi mtima wonse, palibe ndi mmodzi yemwe mwa amuna a zaka makumi awiri kapena kuposa pamenepo, amene anachokera ku Igupto, amene adzaone dziko limene ndinalonjeza mwa lumbiro kwa Abrahamu, Isake ndi Yakobo. 12 Palibe ndi mmodzi yemwe kupatula Kalebe mwana wa Yefune, Mkeni, ndi Yoswa mwana wa Nuni chifukwa anatsatira Yehova ndi mtima wonse.’ 13 Yehova anakwiyira Aisraeli kwambiri ndipo anawachititsa kuyenda mʼchipululu zaka makumi anayi, mpaka mʼbado wonse wa anthu amene anachita choyipa pamaso pake unatha.
14 “Ndipo onani tsopano, inu mʼbado wochimwa, mwalowa mʼmalo mwa makolo anu ndipo mwachititsa kuti Yehova akwiyire Israeli kwambiri. 15 Ngati muleka kumutsata, Iye adzawasiyiranso anthu onsewa mʼchipululu ndipo mudzawonongetsa anthu onsewa.”
16 Ndipo iwo anabwera kwa Mose namuwuza kuti, “Ife tikufuna kumanga makola a ziweto zathu kuno ndi mizinda yokhalamo akazi athu ndi ana athu. 17 Koma ndife okonzeka kutenga zida za nkhondo ndi kupita pamodzi ndi Aisraeli mpaka titakawafikitsa ku malo awo. Panopa, akazi ndi ana athu akhala mʼmizinda yotetezedwa, kuwateteza kwa anthu okhala mʼdzikoli. 18 Sitidzabwerera ku midzi yathu mpaka Mwisraeli aliyense atalandira cholowa chake. 19 Sitidzalandira cholowa chilichonse pamodzi nawo ku tsidya lina la Yorodani, chifukwa cholowa chathu tachipezera ku tsidya lino la kummawa kwa Yorodani.”
20 Tsono Mose anati kwa anthuwo, “Ngati inu mudzachita zimenezi, kutenga zida zankhondo pamaso pa Yehova kuti muchite nkhondo, 21 ndipo ngati nonsenu mudzapita ndi zida kuwoloka Yorodani pamaso pa Yehova mpaka atachotsa adani ake pamaso pake, 22 dzikolo nʼkugonja pamaso pa Yehova, mudzabwera ndi kukhala mfulu pamaso pa Yehova ndi Aisraeli. Ndipo dziko lino lidzakhala lanu pamaso pa Yehova.
23 “Koma mukalephera kuchita izi, mudzakhala mukuchimwira Yehova. Ndipo dziwani kuti tchimo lanu lidzakupezani. 24 Amangireni akazi ndi ana anu mizinda, mangani makola a ziweto zanu, koma chitani zomwe mwalonjeza.”
25 Agadi ndi Arubeni anati kwa Mose, “Ife antchito anu tidzachita monga mbuye wathu mwalamulira. 26 Ana ndi akazi athu, ziweto zathu zina ndi ngʼombe zidzatsala kuno ku mizinda ya Giliyadi, 27 koma antchito anufe, mwamuna aliyense amene ali ndi chida cha nkhondo, adzawoloka kukamenya nkhondo pamaso pa Yehova monga mbuye wathu wanenera.”
28 Choncho Mose anapereka malamulo awa kwa wansembe Eliezara, kwa Yoswa mwana wa Nuni ndi kwa akulu a mafuko a Aisraeli. 29 Mose anawawuza kuti, ngati Agadi ndi Arubeni, mwamuna aliyense wokonzekera nkhondo, awoloka Yorodani pamodzi ndi inu pamaso pa Yehova, ndipo dzikolo nʼkugonjetsedwa pamaso panu, mudzawapatse dziko la Giliyadi kukhala lawo. 30 Koma ngati sawoloka pamodzi nanu ndi zida zankhondo, ayenera kulandira cholowa chawo pamodzi ndi inu ku Kanaani.
31 Agadi ndi Arubeni anayankha kuti, “Antchito anu adzachita zimene Yehova wanena. 32 Tidzawoloka pamaso pa Yehova ndipo tidzalowa mu Kanaani ndi zida zankhondo, koma cholowa chathu chidzakhala ku tsidya lino la Yorodani.”
33 Choncho Mose anapatsa Agadi, Arubeni ndi theka la fuko la Manase mwana wa Yosefe dziko la Sihoni mfumu ya Aamori ndi dziko la Ogi, mfumu ya ku Basani, dziko lonse, mizinda yake ndi midzi yowazungulira.
34 Agadi anamanga Diboni, Ataroti, Aroeri, 35 Atiroti-Sofani, Yazeri, Yogibeha, 36 Beti-Nimira ndi Beti-Harani mizinda ya malinga. Anamanganso makola a ziweto zawo. 37 Ndipo Arubeni anamanga Hesiboni, Eleali, Kiriataimu, 38 Nebo ndi Baala-Meoni (mayina awa anasinthidwa) ndi Sibima. Anapereka mayina ku mizinda ina yomwe anamangayo.
39 Zidzukulu za Makiri mwana wa Manase zinapita ku Giliyadi kulanda mzindawo ndi kuthamangitsira kunja Aamori omwe anali kumeneko. 40 Tsono Mose anapereka Giliyadi kwa Amakiri, ana a Manase, ndipo anakhala kumeneko. 41 Yairi, mwana wa Manase analanda midzi yambiri ya Giliyadi ndi kuyitcha kuti Havoti-Yairi. 42 Ndipo Noba analanda Kenati ndi midzi yozungulira ndi kuyitcha Noba, kutengera dzina la iye mwini.
Numbers 32
New International Version
The Transjordan Tribes
32 The Reubenites and Gadites, who had very large herds and flocks,(A) saw that the lands of Jazer(B) and Gilead(C) were suitable for livestock.(D) 2 So they came to Moses and Eleazar the priest and to the leaders of the community,(E) and said, 3 “Ataroth,(F) Dibon,(G) Jazer,(H) Nimrah,(I) Heshbon,(J) Elealeh,(K) Sebam,(L) Nebo(M) and Beon(N)— 4 the land the Lord subdued(O) before the people of Israel—are suitable for livestock,(P) and your servants have livestock. 5 If we have found favor in your eyes,” they said, “let this land be given to your servants as our possession. Do not make us cross the Jordan.(Q)”
6 Moses said to the Gadites and Reubenites, “Should your fellow Israelites go to war while you sit here? 7 Why do you discourage the Israelites from crossing over into the land the Lord has given them?(R) 8 This is what your fathers did when I sent them from Kadesh Barnea to look over the land.(S) 9 After they went up to the Valley of Eshkol(T) and viewed the land, they discouraged the Israelites from entering the land the Lord had given them. 10 The Lord’s anger was aroused(U) that day and he swore this oath:(V) 11 ‘Because they have not followed me wholeheartedly, not one of those who were twenty years old or more(W) when they came up out of Egypt(X) will see the land I promised on oath(Y) to Abraham, Isaac and Jacob(Z)— 12 not one except Caleb son of Jephunneh the Kenizzite and Joshua son of Nun, for they followed the Lord wholeheartedly.’(AA) 13 The Lord’s anger burned against Israel(AB) and he made them wander in the wilderness forty years, until the whole generation of those who had done evil in his sight was gone.(AC)
14 “And here you are, a brood of sinners, standing in the place of your fathers and making the Lord even more angry with Israel.(AD) 15 If you turn away from following him, he will again leave all this people in the wilderness, and you will be the cause of their destruction.(AE)”
16 Then they came up to him and said, “We would like to build pens(AF) here for our livestock(AG) and cities for our women and children. 17 But we will arm ourselves for battle[a] and go ahead of the Israelites(AH) until we have brought them to their place.(AI) Meanwhile our women and children will live in fortified cities, for protection from the inhabitants of the land. 18 We will not return to our homes until each of the Israelites has received their inheritance.(AJ) 19 We will not receive any inheritance with them on the other side of the Jordan, because our inheritance(AK) has come to us on the east side of the Jordan.”(AL)
20 Then Moses said to them, “If you will do this—if you will arm yourselves before the Lord for battle(AM) 21 and if all of you who are armed cross over the Jordan before the Lord until he has driven his enemies out before him(AN)— 22 then when the land is subdued before the Lord, you may return(AO) and be free from your obligation to the Lord and to Israel. And this land will be your possession(AP) before the Lord.(AQ)
23 “But if you fail to do this, you will be sinning against the Lord; and you may be sure that your sin will find you out.(AR) 24 Build cities for your women and children, and pens for your flocks,(AS) but do what you have promised.(AT)”
25 The Gadites and Reubenites said to Moses, “We your servants will do as our lord commands.(AU) 26 Our children and wives, our flocks and herds will remain here in the cities of Gilead.(AV) 27 But your servants, every man who is armed for battle, will cross over to fight(AW) before the Lord, just as our lord says.”
28 Then Moses gave orders about them(AX) to Eleazar the priest and Joshua son of Nun(AY) and to the family heads of the Israelite tribes.(AZ) 29 He said to them, “If the Gadites and Reubenites, every man armed for battle, cross over the Jordan with you before the Lord, then when the land is subdued before you,(BA) you must give them the land of Gilead as their possession.(BB) 30 But if they do not cross over(BC) with you armed, they must accept their possession with you in Canaan.(BD)”
31 The Gadites and Reubenites answered, “Your servants will do what the Lord has said.(BE) 32 We will cross over before the Lord into Canaan armed,(BF) but the property we inherit will be on this side of the Jordan.(BG)”
33 Then Moses gave to the Gadites,(BH) the Reubenites and the half-tribe of Manasseh(BI) son of Joseph the kingdom of Sihon king of the Amorites(BJ) and the kingdom of Og king of Bashan(BK)—the whole land with its cities and the territory around them.(BL)
34 The Gadites built up Dibon, Ataroth, Aroer,(BM) 35 Atroth Shophan, Jazer,(BN) Jogbehah,(BO) 36 Beth Nimrah(BP) and Beth Haran as fortified cities, and built pens for their flocks.(BQ) 37 And the Reubenites rebuilt Heshbon,(BR) Elealeh(BS) and Kiriathaim,(BT) 38 as well as Nebo(BU) and Baal Meon (these names were changed) and Sibmah.(BV) They gave names to the cities they rebuilt.
39 The descendants of Makir(BW) son of Manasseh went to Gilead,(BX) captured it and drove out the Amorites(BY) who were there. 40 So Moses gave Gilead to the Makirites,(BZ) the descendants of Manasseh, and they settled there. 41 Jair,(CA) a descendant of Manasseh, captured their settlements and called them Havvoth Jair.[b](CB) 42 And Nobah captured Kenath(CC) and its surrounding settlements and called it Nobah(CD) after himself.(CE)
Footnotes
- Numbers 32:17 Septuagint; Hebrew will be quick to arm ourselves
- Numbers 32:41 Or them the settlements of Jair
Numbers 32
New King James Version
The Tribes Settling East of the Jordan(A)
32 Now the children of Reuben and the children of Gad had a very great multitude of livestock; and when they saw the land of (B)Jazer and the land of (C)Gilead, that indeed the region was a place for livestock, 2 the children of Gad and the children of Reuben came and spoke to Moses, to Eleazar the priest, and to the leaders of the congregation, saying, 3 “Ataroth, Dibon, Jazer, (D)Nimrah, (E)Heshbon, Elealeh, (F)Shebam, Nebo, and (G)Beon, 4 the country (H)which the Lord defeated before the congregation of Israel, is a land for livestock, and your servants have livestock.” 5 Therefore they said, “If we have found favor in your sight, let this land be given to your servants as a possession. Do not take us over the Jordan.”
6 And Moses said to the children of Gad and to the children of Reuben: “Shall your brethren go to war while you sit here? 7 Now why will you (I)discourage the heart of the children of Israel from going over into the land which the Lord has given them? 8 Thus your fathers did (J)when I sent them away from Kadesh Barnea (K)to see the land. 9 For (L)when they went up to the Valley of Eshcol and saw the land, they discouraged the heart of the children of Israel, so that they did not go into the land which the Lord had given them. 10 (M)So the Lord’s anger was aroused on that day, and He swore an oath, saying, 11 ‘Surely none of the men who came up from Egypt, (N)from twenty years old and above, shall see the land of which I swore to Abraham, Isaac, and Jacob, because (O)they have not wholly followed Me, 12 except Caleb the son of Jephunneh, the Kenizzite, and Joshua the son of Nun, (P)for they have wholly followed the Lord.’ 13 So the Lord’s anger was aroused against Israel, and He made them (Q)wander in the wilderness forty years, until (R)all the generation that had done evil in the sight of the Lord was gone. 14 And look! You have risen in your fathers’ place, a brood of sinful men, to increase still more the (S)fierce anger of the Lord against Israel. 15 For if you (T)turn away from following Him, He will once again leave them in the wilderness, and you will destroy all these people.”
16 Then they came near to him and said: “We will build sheepfolds here for our livestock, and cities for our little ones, 17 but (U)we ourselves will be armed, ready to go before the children of Israel until we have brought them to their place; and our little ones will dwell in the fortified cities because of the inhabitants of the land. 18 (V)We will not return to our homes until every one of the children of Israel has [a]received his inheritance. 19 For we will not inherit with them on the other side of the Jordan and beyond, (W)because our inheritance has fallen to us on this eastern side of the Jordan.”
20 Then (X)Moses said to them: “If you do this thing, if you arm yourselves before the Lord for the war, 21 and all your armed men cross over the Jordan before the Lord until He has driven out His enemies from before Him, 22 and (Y)the land is subdued before the Lord, then afterward (Z)you may return and be blameless before the Lord and before Israel; and (AA)this land shall be your possession before the Lord. 23 But if you do not do so, then take note, you have sinned against the Lord; and be sure (AB)your sin will find you out. 24 (AC)Build cities for your little ones and folds for your sheep, and do [b]what has proceeded out of your mouth.”
25 And the children of Gad and the children of Reuben spoke to Moses, saying: “Your servants will do as my lord commands. 26 (AD)Our little ones, our wives, our flocks, and all our livestock will be there in the cities of Gilead; 27 (AE)but your servants will cross over, every man armed for war, before the Lord to battle, just as my lord says.”
28 So Moses gave command (AF)concerning them to Eleazar the priest, to Joshua the son of Nun, and to the chief fathers of the tribes of the children of Israel. 29 And Moses said to them: “If the children of Gad and the children of Reuben cross over the Jordan with you, every man armed for battle before the Lord, and the land is subdued before you, then you shall give them the land of Gilead as a possession. 30 But if they do not cross over armed with you, they shall have possessions among you in the land of Canaan.”
31 Then the children of Gad and the children of Reuben answered, saying: “As the Lord has said to your servants, so we will do. 32 We will cross over armed before the Lord into the land of Canaan, but the possession of our inheritance shall remain with us on this side of the Jordan.”
33 So (AG)Moses gave to the children of Gad, to the children of Reuben, and to half the tribe of Manasseh the son of Joseph, (AH)the kingdom of Sihon king of the Amorites and the kingdom of Og king of Bashan, the land with its cities within the borders, the cities of the surrounding country. 34 And the children of Gad built (AI)Dibon and Ataroth and (AJ)Aroer, 35 Atroth and Shophan and (AK)Jazer and Jogbehah, 36 (AL)Beth Nimrah and Beth Haran, (AM)fortified cities, and folds for sheep. 37 And the children of Reuben built (AN)Heshbon and Elealeh and Kirjathaim, 38 (AO)Nebo and (AP)Baal Meon (AQ)(their names being changed) and Shibmah; and they gave other names to the cities which they built.
39 And the children of (AR)Machir the son of Manasseh went to Gilead and took it, and [c]dispossessed the Amorites who were in it. 40 So Moses (AS)gave Gilead to Machir the son of Manasseh, and he dwelt in it. 41 Also (AT)Jair the son of Manasseh went and took its small towns, and called them (AU)Havoth Jair.[d] 42 Then Nobah went and took Kenath and its villages, and he called it Nobah, after his own name.
Footnotes
- Numbers 32:18 possessed
- Numbers 32:24 what you said you would do
- Numbers 32:39 drove out
- Numbers 32:41 Lit. Towns of Jair
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.
Scripture taken from the New King James Version®. Copyright © 1982 by Thomas Nelson. Used by permission. All rights reserved.

