Add parallel Print Page Options

Chipsinjo cha Israeli

Tsoka ine!
Ndili ngati munthu wokunkha zipatso nthawi yachilimwe,
    pa nthawi yokolola mphesa;
palibe phava lamphesa loti nʼkudya,
    palibe nkhuyu zoyambirira zimene ndimazilakalaka kwambiri.
Anthu opembedza atha mʼdziko;
    palibe wolungama ndi mmodzi yemwe amene watsala.
Anthu onse akubisalirana kuti aphane;
    aliyense akusaka mʼbale wake ndi khoka.
Manja awo onse ndi aluso pochita zoyipa;
    wolamulira amafuna mphatso,
woweruza amalandira ziphuphu,
    anthu amphamvu amalamula kuti zichitike zimene akuzifuna,
    onse amagwirizana zochita.
Munthu wabwino kwambiri pakati pawo ali ngati mtengo waminga,
    munthu wolungama kwambiri pakati pawo ndi woyipa kuposa mpanda waminga.
Tsiku limene alonda ako ananena lafika,
    tsiku limene Mulungu akukuchezera.
    Tsopano ndi nthawi ya chisokonezo chawo.
Usadalire mnansi;
    usakhulupirire bwenzi.
Usamale zoyankhula zako
    ngakhale kwa mkazi amene wamukumbatira.
Pakuti mwana wamwamuna akunyoza abambo ake,
    mwana wamkazi akuwukira amayi ake,
mtengwa akukangana ndi apongozi ake,
    adani a munthu ndi amene amakhala nawo mʼbanja mwake momwe.

Koma ine ndikudikira Yehova mwachiyembekezo,
    ndikudikira Mulungu Mpulumutsi wanga;
    Mulungu wanga adzamvetsera.

Kuuka kwa Israeli

Iwe mdani wanga, usandiseke!
    Ngakhale ndagwa, ndidzauka.
Ngakhale ndikukhala mu mdima,
    Yehova ndiye kuwunika kwanga.
Ndidzapirira mkwiyo wa Yehova,
    chifukwa ndinamuchimwira,
mpaka ataweruza mlandu wanga
    ndi kukhazikitsa chilungamo changa.
Iye adzanditulutsa ndi kundilowetsa mʼkuwunika;
    ndidzaona chilungamo chake.
10 Ndipo mdani wanga adzaona zimenezi
    nadzagwidwa ndi manyazi,
iye amene anandifunsa kuti,
    “Ali kuti Yehova Mulungu wako?”
Ndidzaona kugonjetsedwa kwake ndi maso anga;
    ngakhale tsopano adzaponderezedwa
    ngati matope mʼmisewu.

11 Idzafika nthawi yomanganso makoma anu,
    nthawi yokulitsanso malire anu.
12 Nthawi imeneyo anthu adzabwera kwa inu
    kuchokera ku Asiriya ndi mizinda ya ku Igupto,
ngakhale kuchokera ku Igupto mpaka ku Yufurate
    ndiponso kuchokera ku nyanja ina mpaka ku nyanja inanso
    kuchokera ku phiri lina mpaka ku phiri linanso.
13 Dziko lapansi lidzasanduka chipululu
    chifukwa cha anthu okhala mʼdzikomo, potsatira zochita za anthuwo.

Pemphero ndi Matamando

14 Wetani anthu anu ndi ndodo yanu yowateteza,
    nkhosa zimene ndi cholowa chanu,
zimene zili zokha mʼnkhalango,
    mʼdziko la chonde.
Muzilole kuti zidye mu Basani ndi mu Giliyadi
    monga masiku akale.

15 “Ndidzawaonetsa zodabwitsa zanga,
    ngati masiku amene ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto.”

16 Mitundu ya anthu idzaona zimenezi ndipo idzachita manyazi,
    ngakhale ali ndi mphamvu zotani.
Adzagwira pakamwa pawo
    ndipo makutu awo adzagontha.
17 Adzabwira fumbi ngati njoka,
    ngati zolengedwa zomwe zimakwawa pansi.
Adzabwera akunjenjemera kuchokera mʼmaenje awo;
    mwamantha adzatembenukira kwa Yehova Mulungu wathu
    ndipo adzachita nanu mantha.
18 Kodi alipo Mulungu wofanana nanu,
    amene amakhululukira tchimo ndi kuyiwala zolakwa
    za anthu otsala amene ndi cholowa chake?
Inu simusunga mkwiyo mpaka muyaya
    koma kwanu nʼkuonetsa chikondi chosasinthika.
19 Inu mudzatichitiranso chifundo;
    mudzapondereza pansi machimo athu
    ndi kuponyera zolakwa zathu zonse pansi pa nyanja.
20 Mudzakhala wokhulupirika kwa Yakobo,
    ndi kuonetsa chifundo chanu kwa Abrahamu,
monga munalonjeza molumbira kwa makolo athu
    masiku amakedzana.

Israel’s Misery

What misery is mine!
I am like one who gathers summer fruit
    at the gleaning of the vineyard;
there is no cluster of grapes to eat,
    none of the early figs(A) that I crave.
The faithful have been swept from the land;(B)
    not one(C) upright person remains.
Everyone lies in wait(D) to shed blood;(E)
    they hunt each other(F) with nets.(G)
Both hands are skilled in doing evil;(H)
    the ruler demands gifts,
the judge accepts bribes,(I)
    the powerful dictate what they desire—
    they all conspire together.
The best of them is like a brier,(J)
    the most upright worse than a thorn(K) hedge.
The day God visits you has come,
    the day your watchmen sound the alarm.
    Now is the time of your confusion.(L)
Do not trust a neighbor;
    put no confidence in a friend.(M)
Even with the woman who lies in your embrace
    guard the words of your lips.
For a son dishonors his father,
    a daughter rises up against her mother,(N)
a daughter-in-law against her mother-in-law—
    a man’s enemies are the members of his own household.(O)

But as for me, I watch(P) in hope(Q) for the Lord,
    I wait for God my Savior;
    my God will hear(R) me.

Israel Will Rise

Do not gloat over me,(S) my enemy!
    Though I have fallen, I will rise.(T)
Though I sit in darkness,
    the Lord will be my light.(U)
Because I have sinned against him,
    I will bear the Lord’s wrath,(V)
until he pleads my case(W)
    and upholds my cause.
He will bring me out into the light;(X)
    I will see his righteousness.(Y)
10 Then my enemy will see it
    and will be covered with shame,(Z)
she who said to me,
    “Where is the Lord your God?”(AA)
My eyes will see her downfall;(AB)
    even now she will be trampled(AC) underfoot
    like mire in the streets.

11 The day for building your walls(AD) will come,
    the day for extending your boundaries.
12 In that day people will come to you
    from Assyria(AE) and the cities of Egypt,
even from Egypt to the Euphrates
    and from sea to sea
    and from mountain to mountain.(AF)
13 The earth will become desolate because of its inhabitants,
    as the result of their deeds.(AG)

Prayer and Praise

14 Shepherd(AH) your people with your staff,(AI)
    the flock of your inheritance,
which lives by itself in a forest,
    in fertile pasturelands.[a](AJ)
Let them feed in Bashan(AK) and Gilead(AL)
    as in days long ago.(AM)

15 “As in the days when you came out of Egypt,
    I will show them my wonders.(AN)

16 Nations will see and be ashamed,(AO)
    deprived of all their power.
They will put their hands over their mouths(AP)
    and their ears will become deaf.
17 They will lick dust(AQ) like a snake,
    like creatures that crawl on the ground.
They will come trembling(AR) out of their dens;
    they will turn in fear(AS) to the Lord our God
    and will be afraid of you.
18 Who is a God(AT) like you,
    who pardons sin(AU) and forgives(AV) the transgression
    of the remnant(AW) of his inheritance?(AX)
You do not stay angry(AY) forever
    but delight to show mercy.(AZ)
19 You will again have compassion on us;
    you will tread our sins underfoot
    and hurl all our iniquities(BA) into the depths of the sea.(BB)
20 You will be faithful to Jacob,
    and show love to Abraham,(BC)
as you pledged on oath to our ancestors(BD)
    in days long ago.(BE)

Footnotes

  1. Micah 7:14 Or in the middle of Carmel