Masalimo 75
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.
75 Tikuthokoza Inu Mulungu,
tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,
anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.
2 Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,
ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
3 Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,
ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.
Sela
4 Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’
ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
5 Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;
musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”
6 Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo
kapena ku chipululu.
7 Koma ndi Mulungu amene amaweruza:
Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
8 Mʼdzanja la Yehova muli chikho
chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;
Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi
amamwa ndi senga zake zonse.
9 Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;
ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa
koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.
Psalm 75
New International Version
Psalm 75[a]
For the director of music. To the tune of “Do Not Destroy.” A psalm of Asaph. A song.
1 We praise you, God,
we praise you, for your Name is near;(A)
people tell of your wonderful deeds.(B)
2 You say, “I choose the appointed time;(C)
it is I who judge with equity.(D)
3 When the earth and all its people quake,(E)
it is I who hold its pillars(F) firm.[b]
4 To the arrogant(G) I say, ‘Boast no more,’(H)
and to the wicked, ‘Do not lift up your horns.[c](I)
5 Do not lift your horns against heaven;
do not speak so defiantly.(J)’”
6 No one from the east or the west
or from the desert can exalt themselves.
7 It is God who judges:(K)
He brings one down, he exalts another.(L)
8 In the hand of the Lord is a cup
full of foaming wine mixed(M) with spices;
he pours it out, and all the wicked of the earth
drink it down to its very dregs.(N)
Footnotes
- Psalm 75:1 In Hebrew texts 75:1-10 is numbered 75:2-11.
- Psalm 75:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
- Psalm 75:4 Horns here symbolize strength; also in verses 5 and 10.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.
Holy Bible, New International Version®, NIV® Copyright ©1973, 1978, 1984, 2011 by Biblica, Inc.® Used by permission. All rights reserved worldwide.
NIV Reverse Interlinear Bible: English to Hebrew and English to Greek. Copyright © 2019 by Zondervan.