Add parallel Print Page Options

Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe, potsata mayimbidwe a “Musawononge.” Salimo la Asafu. Nyimbo.

75 Tikuthokoza Inu Mulungu,
    tikuthokoza, pakuti dzina lanu lili pafupi nafe,
    anthutu amafotokoza za ntchito zanu zodabwitsa.

Mumati, “Ine ndimayika nthawi yoyenera,
    ndine amene ndimaweruza mwachilungamo.
Pamene dziko lapansi ndi anthu ake onse anjenjemera,
    ndine amene ndimagwiriziza mizati yake molimba.
            Sela
Kwa odzitama ndikuti, ‘Musadzitamenso,’
    ndipo kwa oyipa, ‘Musatukulenso nyanga zanu.
Musatukule nyanga zanu motsutsana ndi kumwamba;
    musayankhule ndi khosi losololoka.’ ”

Kugamula milandu sikuchokera kummawa kapena kumadzulo
    kapena ku chipululu.
Koma ndi Mulungu amene amaweruza:
    Iyeyo amatsitsa wina, nakwezanso wina.
Mʼdzanja la Yehova muli chikho
    chodzaza ndi vinyo wochita thovu, wosakanizidwa ndi zokometsera;
Iye amamutsanulira pansi ndipo onse oyipa a dziko lapansi
    amamwa ndi senga zake zonse.

Kunena za ine, ndidzalengeza izi kwamuyaya;
    ndidzayimba matamando kwa Mulungu wa Yakobo.
10 Ndidzadula nyanga za onse oyipa
    koma nyanga za olungama zidzakwezedwa.

Psalm 75[a]

For the director of music. To the tune of “Do Not Destroy.” A psalm of Asaph. A song.

We praise you, God,
    we praise you, for your Name is near;(A)
    people tell of your wonderful deeds.(B)

You say, “I choose the appointed time;(C)
    it is I who judge with equity.(D)
When the earth and all its people quake,(E)
    it is I who hold its pillars(F) firm.[b]
To the arrogant(G) I say, ‘Boast no more,’(H)
    and to the wicked, ‘Do not lift up your horns.[c](I)
Do not lift your horns against heaven;
    do not speak so defiantly.(J)’”

No one from the east or the west
    or from the desert can exalt themselves.
It is God who judges:(K)
    He brings one down, he exalts another.(L)
In the hand of the Lord is a cup
    full of foaming wine mixed(M) with spices;
he pours it out, and all the wicked of the earth
    drink it down to its very dregs.(N)

As for me, I will declare(O) this forever;
    I will sing(P) praise to the God of Jacob,(Q)
10 who says, “I will cut off the horns of all the wicked,
    but the horns of the righteous will be lifted up.”(R)

Footnotes

  1. Psalm 75:1 In Hebrew texts 75:1-10 is numbered 75:2-11.
  2. Psalm 75:3 The Hebrew has Selah (a word of uncertain meaning) here.
  3. Psalm 75:4 Horns here symbolize strength; also in verses 5 and 10.