Add parallel Print Page Options

Chikondi cha Mulungu pa Israeli

11 “Israeli ali mwana, ndinamukonda,
    ndipo ndinayitana mwana wanga kuti atuluke mu Igupto.
Koma ndimati ndikamapitiriza kuyitana
    iwo amandithawa kupita kutali.
Ankapereka nsembe kwa Abaala
    ndipo ankafukiza lubani kwa mafano.
Ndi Ine amene ndinaphunzitsa Efereimu kuyenda,
    ndipo ndinawagwira pa mkono;
koma iwo sanazindikire
    kuti ndine amene ndinawachiritsa.
Ndinawatsogolera ndi zingwe zachifundo cha anthu
    ndi zomangira za chikondi;
ndinachotsa goli mʼkhosi mwawo
    ndipo ndinawerama nʼkuwadyetsa.

“Sadzabwerera ku Igupto,
    koma Asiriya ndiye adzakhala mfumu yawo
    pakuti akana kutembenuka.
Malupanga adzangʼanima mʼmizinda yawo,
    ndipo adzawononga mipiringidzo ya zipata zawo
    nadzathetseratu malingaliro awo.
Anthu anga atsimikiza zondifulatira Ine.
    Ngakhale atayitana Wammwambamwamba,
    sizidzatheka kuti Iye awakwezenso.

“Kodi ndingakusiye bwanji iwe Efereimu?
    Kodi ndingakupereke bwanji iwe Israeli?
Kodi ndingakuchitire bwanji zimene ndinachitira Adima?
    Kodi ndingathe bwanji kukuchitira zimene ndinachitira Zeboimu?
Mtima wanga wakana kutero;
    chifundo changa chonse chikusefukira.
Sindidzalola kuti ndikulange ndi mkwiyo wanga woopsa,
    kapena kutembenuka ndi kuwononga Efereimu.
Pakuti Ine ndine Mulungu osati munthu,
    Woyerayo pakati panu.
    Sindidzabwera mwaukali.
10 Iwo adzatsatira Yehova;
    Iye adzabangula ngati mkango.
Akadzabangula,
    ana ake adzabwera akunjenjemera kuchokera kumadzulo.
11 Adzabwera akunjenjemera
    ngati mbalame kuchokera ku Igupto,
    ngati nkhunda kuchokera ku Asiriya.
Ine ndidzawakhazikanso mʼnyumba zawo,”
    akutero Yehova.

Tchimo la Israeli

12 Efereimu wandizungulira ndi mabodza,
    nyumba ya Israeli yandizungulira ndi chinyengo.
Ndipo Yuda wawukira Mulungu,
    wawukira ngakhale Woyerayo amene ndi wokhulupirika.

God’s Love for Israel

11 “When Israel was a child,(A) I loved(B) him,
    and out of Egypt I called my son.(C)
But the more they were called,
    the more they went away from me.[a](D)
They sacrificed to the Baals(E)
    and they burned incense to images.(F)
It was I who taught Ephraim to walk,
    taking them by the arms;(G)
but they did not realize
    it was I who healed(H) them.
I led them with cords of human kindness,
    with ties of love.(I)
To them I was like one who lifts
    a little child to the cheek,
    and I bent down to feed(J) them.(K)

“Will they not return to Egypt(L)
    and will not Assyria(M) rule over them
    because they refuse to repent?(N)
A sword(O) will flash in their cities;
    it will devour(P) their false prophets
    and put an end to their plans.
My people are determined to turn(Q) from me.(R)
    Even though they call me God Most High,
    I will by no means exalt them.

“How can I give you up,(S) Ephraim?(T)
    How can I hand you over, Israel?
How can I treat you like Admah?
    How can I make you like Zeboyim?(U)
My heart is changed within me;
    all my compassion(V) is aroused.(W)
I will not carry out my fierce anger,(X)
    nor will I devastate(Y) Ephraim again.
For I am God, and not a man(Z)
    the Holy One(AA) among you.
    I will not come against their cities.
10 They will follow the Lord;
    he will roar(AB) like a lion.(AC)
When he roars,
    his children will come trembling(AD) from the west.(AE)
11 They will come from Egypt,
    trembling like sparrows,
    from Assyria,(AF) fluttering like doves.(AG)
I will settle them in their homes,”(AH)
    declares the Lord.

Israel’s Sin

12 Ephraim has surrounded me with lies,(AI)
    Israel with deceit.
And Judah is unruly against God,
    even against the faithful(AJ) Holy One.[b](AK)

Footnotes

  1. Hosea 11:2 Septuagint; Hebrew them
  2. Hosea 11:12 In Hebrew texts this verse (11:12) is numbered 12:1.