Add parallel Print Page Options

Ana ndi Makolo Awo

Inu ana, mverani makolo anu mwa Ambuye, pakuti zimenezi ndi zoyenera. “Lemekeza abambo ndi amayi ako.” Limeneli ndi lamulo loyamba lokhala ndi lonjezo. Ngati ulemekeza abambo ako ndi amayi ako, “zinthu zidzakuyendera bwino ndipo udzasangalala ndi moyo wautali pa dziko lapansi.” Abambo musakwiyitse ana anu; mʼmalo mwake, muwalere mʼchiphunzitso ndi mʼchilangizo cha Ambuye.

Antchito ndi Mabwana Awo

Inu antchito, mverani mabwana anu mwaulemu ndi mwamantha ndi moona mtima, monga momwe mungamvere Khristu. Musawamvere pamene akukuonani kuti akukomereni mtima, koma ngati akapolo a Khristu ochita chifuniro cha Mulungu kuchokera mu mtima mwanu. Tumikirani ndi mtima wonse, ngati kuti mukutumikira Ambuye, osati anthu. Inu mukudziwa kuti Ambuye adzamupatsa munthu aliyense mphotho chifukwa cha ntchito yake yabwino imene anagwira, kaya munthuyo ndi kapolo kapena mfulu.

Ndipo inu mabwana, muziwachitiranso chimodzimodzi antchito anu. Musamawaopseze, popeza mukudziwa kuti Mbuye wawo ndi wanunso, nonse Mbuye wanu ali kumwamba, ndipo Iyeyo alibe tsankho.

Zida Zankhondo za Mulungu

10 Potsiriza ndikuti, dzilimbitseni mwa Ambuye ndi mwa mphamvu zake zazikulu. 11 Valani zida zonse za Mulungu kuti muthe kuyima ndi kukana machenjerero a Satana. 12 Pakuti sitikulimbana ndi thupi ndi magazi, koma tikulimbana ndi maufumu, maulamuliro, mphamvu za dziko la mdima, ndi mphamvu zoyipa kwambiri zauzimu zamlengalenga. 13 Choncho valani zida zonse za Mulungu, kuti pamene tsiku loyipa kwambiri lifika, mudzathe kuyima chilili, ndipo mutatha kuchita zonse, mudzayimabe mwamphamvu. 14 Tsono imani mwamphamvu, mutamangira choonadi ngati lamba mʼchiwuno mwanu, mutavala chilungamo ngati chitsulo chotchinjiriza pa chifuwa. 15 Valani Uthenga Wabwino wamtendere ku mapazi anu ngati nsapato. 16 Kuwonjezera pa zonsezi, nyamulani chishango cha chikhulupiriro, ndipo ndi chimenechi mudzatha kuzimitsa mivi yonse yoyaka moto ya oyipayo. 17 Valani chipewa cha chipulumutso ndi kutenga lupanga la mzimu, limene ndi Mawu a Mulungu. 18 Ndipo mupemphere mwa Mzimu nthawi zonse, mʼmitundu yonse ya mapemphero ndi zopempha. Ndipo pozindikira izi, khalani achangu kupempherera oyera mtima nthawi zonse.

19 Mundipempherere inenso, kuti nthawi iliyonse pamene nditsekula pakamwa panga, andipatse mawu kuti ndiwulule zinsinsi za Uthenga Wabwino mopanda mantha. 20 Ndine kazembe wa Uthenga Wabwinowu ngakhale ndili womangidwa mʼndende. Pempherani kuti ndilalikire mopanda mantha, monga ndiyenera.

Mawu Otsiriza

21 Tukiko, mʼbale wanga wokondedwa ndi mtumiki wokhulupirika mwa Ambuye, adzakuwuzani zonse kuti inunso mudziwe mmene ndilili ndi zimene ndikuchita. 22 Ine ndikumutumiza kwa inu, kuti mudziwe za moyo wathu, ndi kuti akulimbikitseni.

23 Mtendere, chikondi pamodzi ndi chikhulupiriro kuchokera kwa Mulungu Atate ndi Ambuye Yesu Khristu zikhale ndi abale onse. 24 Chisomo kwa onse amene amakonda Ambuye athu Yesu Khristu ndi chikondi chosatha.

Children, obey your parents in the Lord, for this is right.(A) “Honor your father and mother”—which is the first commandment with a promise— “so that it may go well with you and that you may enjoy long life on the earth.”[a](B)

Fathers,[b] do not exasperate your children;(C) instead, bring them up in the training and instruction of the Lord.(D)

Slaves, obey your earthly masters with respect(E) and fear, and with sincerity of heart,(F) just as you would obey Christ.(G) Obey them not only to win their favor when their eye is on you, but as slaves of Christ,(H) doing the will of God from your heart. Serve wholeheartedly, as if you were serving the Lord, not people,(I) because you know that the Lord will reward each one for whatever good they do,(J) whether they are slave or free.

And masters, treat your slaves in the same way. Do not threaten them, since you know that he who is both their Master and yours(K) is in heaven, and there is no favoritism(L) with him.

The Armor of God

10 Finally, be strong in the Lord(M) and in his mighty power.(N) 11 Put on the full armor of God,(O) so that you can take your stand against the devil’s schemes. 12 For our struggle is not against flesh and blood,(P) but against the rulers, against the authorities,(Q) against the powers(R) of this dark world and against the spiritual forces of evil in the heavenly realms.(S) 13 Therefore put on the full armor of God,(T) so that when the day of evil comes, you may be able to stand your ground, and after you have done everything, to stand. 14 Stand firm then, with the belt of truth buckled around your waist,(U) with the breastplate of righteousness in place,(V) 15 and with your feet fitted with the readiness that comes from the gospel of peace.(W) 16 In addition to all this, take up the shield of faith,(X) with which you can extinguish all the flaming arrows of the evil one.(Y) 17 Take the helmet of salvation(Z) and the sword of the Spirit,(AA) which is the word of God.(AB)

18 And pray in the Spirit(AC) on all occasions(AD) with all kinds of prayers and requests.(AE) With this in mind, be alert and always keep on praying(AF) for all the Lord’s people. 19 Pray also for me,(AG) that whenever I speak, words may be given me so that I will fearlessly(AH) make known the mystery(AI) of the gospel, 20 for which I am an ambassador(AJ) in chains.(AK) Pray that I may declare it fearlessly, as I should.

Final Greetings

21 Tychicus,(AL) the dear brother and faithful servant in the Lord, will tell you everything, so that you also may know how I am and what I am doing. 22 I am sending him to you for this very purpose, that you may know how we are,(AM) and that he may encourage you.(AN)

23 Peace(AO) to the brothers and sisters,[c] and love with faith from God the Father and the Lord Jesus Christ. 24 Grace to all who love our Lord Jesus Christ with an undying love.[d]

Footnotes

  1. Ephesians 6:3 Deut. 5:16
  2. Ephesians 6:4 Or Parents
  3. Ephesians 6:23 The Greek word for brothers and sisters (adelphoi) refers here to believers, both men and women, as part of God’s family.
  4. Ephesians 6:24 Or Grace and immortality to all who love our Lord Jesus Christ.