Masalimo 26
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Davide.
26 Weruzeni Inu Yehova
pakuti ndakhala moyo wosalakwa.
Ndadalira Yehova
popanda kugwedezeka.
2 Patseni mayeso, Inu Yehova ndipo ndiyeseni,
santhulani mtima wanga ndi maganizo anga;
3 pakuti chikondi chanu chili pamaso panga nthawi zonse,
ndipo ndimayenda mʼchoonadi chanu nthawi zonse.
4 Ine sindikhala pansi pamodzi ndi anthu achinyengo,
kapena kufunsa nzeru kwa achiphamaso.
5 Ndimanyansidwa ndi msonkhano wa anthu ochita zoyipa
ndipo ndimakana kukhala pansi pamodzi ndi oyipa.
6 Ndimasamba mʼmanja mwanga kuonetsa kusalakwa kwanga
ndi kupita kukatumikira pa guwa lanu la nsembe, Inu Yehova,
7 kulengeza mofuwula za matamando anu
ndi kuwuza onse za ntchito zanu zodabwitsa.
8 Ndimakonda Nyumba imene Inu Yehova mumakhalamo,
malo amene ulemerero wanu umapezekako.
9 Musachotse moyo wanga pamodzi ndi ochimwa,
moyo wanga pamodzi ndi anthu akupha anzawo,
10 amene mʼmanja mwawo muli ndondomeko zoyipa,
dzanja lawo lamanja ladzaza ndi ziphuphu.
11 Koma ine ndimakhala moyo wosalakwa;
mu msonkhano wa anthu anu ndidzatamanda Yehova.
12 Ndayima pa malo wopanda zovuta
ndipo ndidzatamanda Yehova mu msonkhano waukulu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.