Masalimo 46
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Ndakatulo ya ana a Kora. Nyimbo ya anamwali.
46 Mulungu ndiye kothawira kwathu ndi mphamvu yathu,
thandizo lopezekeratu pa nthawi ya mavuto.
2 Nʼchifukwa chake sitidzaopa ngakhale dziko lapansi lisunthike,
ngakhale mapiri agwe pakati pa nyanja,
3 ngakhale madzi ake atakokoma ndi kuchita thovu,
ngakhale mapiri agwedezeke ndi kukokoma kwake.
4 Kuli mtsinje umene njira zake za madzi zimasangalatsa mzinda wa Mulungu,
malo oyera kumene Wammwambamwamba amakhalako.
5 Mulungu ali mʼkati mwake, iwo sudzagwa;
Mulungu adzawuthandiza mmawa.
6 Mitundu ikupokosera, mafumu akugwa;
Iye wakweza mawu ake, dziko lapansi likusungunuka.
7 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,
Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
8 Bwerani kuti mudzaone ntchito za Yehova,
chiwonongeko chimene wachibweretsa pa dziko lapansi.
9 Iye amathetsa nkhondo ku malekezero a dziko lapansi;
Iye amathyola uta ndi kupindapinda mkondo;
amatentha zishango ndi moto.
10 Iye akuti, “Khala chete, ndipo dziwa kuti ndine Mulungu;
ndidzakwezedwa pakati pa mitundu ya anthu;
ine ndidzakwezedwa mʼdziko lapansi.”
11 Yehova Wamphamvuzonse ali ndi ife,
Mulungu wa Yakobo ndi linga lathu.
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.