Masalimo 24
Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero
Salimo la Davide.
24 Dziko lapansi ndi la Yehova ndi zonse zimene zili mʼmenemo,
dziko ndi onse amene amakhala mʼmenemo;
2 pakuti Iye ndiye anayika maziko ake pa nyanja
ndi kulikhazika pamwamba pa madzi.
3 Ndani angakwere phiri la Yehova?
Ndani angathe kuyima pa malo ake opatulika?
4 Iye amene ali ndi mʼmanja moyera ndi mtima woyera,
amene sapereka moyo wake kwa fano
kapena kulumbira mwachinyengo.
5 Iyeyo adzalandira madalitso kwa Yehova
ndipo Mulungu mpulumutsi wake adzagamula kuti alibe mlandu.
6 Umenewo ndiwo mʼbado wa amene amafunafuna Yehova;
amene amafunafuna nkhope yanu, Inu Mulungu wa Yakobo.
Sela
7 Tukulani mitu yanu inu zipata;
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
8 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
Yehova Wamphamvuzonse,
Yehova ndiye wamphamvu pa nkhondo.
9 Tukulani mitu yanu, inu zipata;
tsekukani, inu zitseko zakalekalenu,
kuti Mfumu yaulemerero ilowe.
10 Kodi Mfumu yaulemereroyo ndani?
Yehova Wamphamvuzonse,
Iye ndiye Mfumu yaulemerero.
Sela
The Word of God in Contemporary Chichewa Copyright © 2002, 2016 by Biblica, Inc.® Used by permission of Biblica, Inc.® All rights reserved worldwide. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Mwini © 2002, 2016 ndi Biblica, Inc.® Kugwiritsa ntchito mwachilolezo. Umwini ndi otetezedwa pa dziko lonse.